/1 Koma Mulungu atsimikiza kwa ife cikondi cace ca mwini yekha m'menemo, kuti pokhala ife cikhalire ocimwa, Kristu adatifera ife. Koma pasanafike phwando la Paskha, Yesu, podziwa kuti nthawi yace idadza yakucoka kuturuka m'dziko lino lapansi, kunka kwa Atate, m'mene anakonda ace a Iye yekha a m'dziko lapansi, anawakonda kufikira cimariziro. Ndi kwa Yesu Kristu, mboni yokhulupirikayo, wobadwa woyamba wa akufa, ndi mkulu wa mafumu a dziko lapansi; Kwa Iye amene atikonda ife, natimasula ku macimo athu ndi mwazi wace. Yehova anaonekera kwa ine kale, ndi kuti, Inde, ndakukonda iwe ndi cikondi cosatha; cifukwa cace ndakukoka iwe ndi kukukomera mtima. Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wace wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira Iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha. /2 Yesu ananena naye, Kodi ndiri ndi inu nthawi yaikuru yotere, ndipo sunandizindikira, Filipo? Iye amene wandiona Ine waona Atate; unena iwe bwanji, Mutionetsere Atate?. Sukhulupirira kodi kuti ndiri Ine mwa Atate, ndi Atate ali mwa Ine?.